Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Phunziro 6

Phunziro 6

Tayang’ana zala zako za m’manjazo ndipo ugwedeze zala zako za kumiyendo.

Loza makutu ako, kenako uloze mphuno yako.

Tayang’ana miyendo yakoyo. Miyendo imeneyi ndi yomwe imakuthandiza kuti uzitha kuthamanga, kudumpha, kupanga masewera ozungulira ndi masewera ena osiyanasiyana.

Yang’ana pagalasi. Kodi ukuona chiyani?

Zonse zimene Yehova anapanga n’zabwino kwambiri.

ZOTI MUCHITE

Mwana wanuyo muwerengereni:

Salimo 139:14

Muuzeni mwanayo kuti aloze:

Zala zake zam’manja Zala zake zakumiyendo Mphuno yake

Makutu ake Pakamwa pake

Pezani zinthu zobisika.

Nkhanu Mphaka

Mufunseni mwana wanu kuti:

Kodi ndani analenga iweyo ndi ine?